Prayers & Meditations

Chichewa · Bahá'u'lláh

Add range:

(Mapemphero ili limawerengedwa pa Manda a Bahá’u’lláh ndi Báb. Limagwiritsidwanso ntchito pokumbukira kubadwa kwa Bahá’u’lláh ndi Báb komanso kukumbukira kuwera kumwamba kwa Bahá’u’lláh ndi kuphedwa kwa Báb)

Mayamiko amene m’bandakucha wake waonekera ndi nkhope Yanu yolemekezeka kopambana, ndi ulemelero umene wawala kuchokera kwa Wokongola mowala kopambana, akhale pa Inu, O Inu Amene Muli Maonekedwe a Ulemelero, ndi Mfumu Yamuyaya, ndi Ambuye wa onse amene ali m’mwamba ndi padziko lapansi!

Ine nditsimikiza kuti kupyolera mwa Inu Ufumu wa Mulungu ndi Ukulu wa Mulungu ndi Ulemelero Wake, zinabvumbulutsidwa, ndipo nthanda za kunyezimira Kwake kwakale-kale zagwetsa kuwala kwao kumwamba kwa lamulo Lanu losasinthika, ndipo kukongola kwa Wosaonekayo kwawala pamwamba pa zolengedwa zonse.

Nditsimikizanso kuti ndi kuyenda kwa Cholembera Chanu Chokha, Chifuniro Chanu chakuti: “Khala Iwe” chakwaniritsidwa, ndiponso chinsinsi cha Mulungu chaululidwa, ndipo zinthu zonse zolengedwa zaitanidwa kumoyo ndi Zibvumbulutso zonse zatsika pansi.

Ine ndichitira umboninso, kuti kupyolera mwa kukongola Kwanu, Kukongola kwa Wopembedzayo kwaonetsedwa, ndipo kupyolera mwa Nkhope Yanu, Nkhope ya Wofunikayo Yawala, ndi kuti kupyolera mwa mau Anu, Inu mwaganizira bwino pakati pa zolengedwa zonse, kuwapangitsa amene ali wopembedza Inu kukwera ku nsonga ya ulemelero, ndi wosakhulupilira kugwera m’mbuna yakuya.

Ine ndichitira umboni kuti iye amene wakudziwani Inu wadziwa Mulungu, ndi iye amene wafika pamaso Panu wafika pamaso pa Mulungu. Chomwecho nkwakukulu kudalitsidwa kwa iye amene wakhulupilira mwa Inu, ndi mwa zizindikiro Zanu, ndipo walemekezedwa ndi kukomana Nanu, ndipo wafika pa zokoma za chifuniro Chanu, ndi kukuzungulirani ndi kuima patsogolo pa Mpando Wanu.

Tsoka kwa iye amene wakulakwirani Inu, ndipo wakukanani Inu, ndipo sanabvomera zizindikiro Zanu, ndipo watsutsa ufumu Wanu, ndipo wakuukirani Inu, ndipo wasonyeza kunyada pamaso Panu, ndipo wakangana ndi maumboni Anu, ndipo wathawa chilamulo Chanu ndi ulamuliro Wanu ndi kuwerengedwa limodzi ndi wosakhulupilira amene maina awo asindikizidwa ndi zala za kulamula Kwanu pamauthenga Anu oyera.

Chomwecho, uzirani kwa ine, O Mulungu wanga ndi Wokondedwa wanga, kuchokera kudzanja lamanja la chifundo Chanu ndi chisoni cha kukonda Kwanu, mphweya woyera wa ubwino Wanu, kuti zindichotse ine ndekha ndi m’dziko lapansi ndi kunditengera ku mabwalo a kuyandikira kwanu ndi pamaso Panu. Muli ndi mphamvu kuchita zomwe zakukomerani. Inu ndithudi Mwakhala Wamphamvu koposa zonse.

Chikumbukiro cha Mulungu ndi mayamiko Ache, ndi Ulemelero wa Mulungu ndi kuwala kwake zikhale pa Inu, O Inu Amene Muli kukongola Kwake! Ndichitira umboni kuti diso la chilengedwe silinaone wina wolakwiridwa monga Inu. Munamizidwa masiku onse amoyo Wanu pansi pa nyanja ya zowawa. Pa nthawi yina Munali m’maunyolo ndi nsinga; pa nthawi yinanso Munaopsezedwa ndi lupanga la adani Anu. Komabe, ngakhale ziri chomwecho munalamulira wanthu onse kutsata zonse zimene Munalangizidwa ndi Iye Amene Ali Wodziwa Zonse, Wanzeru Zonse.

Lolani mzimu wanga ukhale nsembe chifukwa cha zolakwa zimene Inu Munabvutika nazo ndi moyo wanga ukhale chopereka chifukwa cha mikwingwirima yomwe Munapwetekedwa nayo. Ndipempha Mulungu,mwa Inu ndi mwa iwo amene nkhope zawo zawalitsidwa ndi kuunika kwa Nkhope Yanu, ndi iwo amene, chifukwa cha chikondi Chanu, atsata zonse zimene anafunsidwa, kuchotsa zophimba zomwe zabwera pakati pa Inu ndi zolengedwa Zanu, ndi kundipatsa ine zabwino padziko lino ndi dziko lirinkudza. Inu zoonadi Ndinu

Wamphamvu Zonse, Wam’mwamba-mwamba, Woyerayera, Wokhululukira Nthawi Zonse, Wachifundo Chozama.

Dalitsani, O Ambuye Ambuye wanga, Mtengo Wopatulika wa Lote ndi masamba ake, ndi makungwa ake ndi nthambi zake, ndi misinde yake ndi mphukira zake malingana ndi momwe maina Anu opambana adzakhalira ndi maudindo Anu wotchuka kwambiri adzatha. Uchinjilizeni chomwecho kuchokera ku zokhumudwitsa za achiwembu ndi magulu ankhanza.

Inu Ndinu, zoonadi Wamphamvu Zonse, Wolimba Kwambiri. Dalitsaninso, O Ambuye Mulungu wanga, antchito Anu ndi adzakazi Anu amene afika kwa Inu. Inu zoonadi Ndinu Wachifundo Chonse, amene chisomo Chake m’chamuyaya. Palibe Mulungu wina koma Inu, Wokhululukira-nthawi Zonse, Wokomamtima.

Iye amene afuna kunena Pempheroli, ayenera kuyimirira ndipo atembenukire kwa Mulungu, ndipo poimirira pamalo akewo, iye ayang’ane kudzanja lamanja ndi lamanzere, ngati kuti akuyembekezera chifundo cha Ambuye Wake, Wachifundo-Choposa, Womvera Chisoni. Tsono iye anene kuti:

O Inu Amene muli Ambuye wamaina onse ndi Mlengi wa miyamba! Ndikupemphani Inu kubzolera mwa iwo Amene ali kasupe a Uweniweni Wanu osaonekawo, Wokwezeka koposa, Waulemelero Onse, kuti mulipange pemphero langa, moto umene uwotche zophimba zimene zanditseka ine kuti ndisaone kukongola Kwanu, ndi kuwala kumene kunditsogolere ine ku nyanja ya kumene Inu Mukupezeka.

Kenaka iye akweze manja ake mopempha kulozera kwa Mulungu -wodalitsika ndi wokwezeka ndi Iye – ndipo anene:

O Inu Khumbo la dziko lapansi ndi Okondedwa wa amitundu! Inu mukundiwona ine ndikutembenukira kwa Inu, ndikudzilekanitsa kwa aliyense kupatula Inu, ndi kukakamira ku chingwe Chanu, chomwe kubzolera mu mayendedwe ake chilengedwe chonse chawongoleredwa.

Ndine mtumiki Wanu, O Ambuye wanga ndiponso mwana wa mtumiki Wanu. Onani ine ndili chilili kukonzekera kuchita Chifuniro Chanu ndiponso khumbo Lanu, ndi kusafuna china chilichonse kupatula chikondwerero Chanu chokoma. Ndikudandaulirani kubzolera m’nyanja ya chifundo Chanu ndi Nyenyezi ya Nthanda ya chisomo Chanu kuti muchite naye mtumiki Wanu monga momwe mufunira ndi kusangalatsidwira. Mwa nyonga zanu zomwe zili patali popitilira kutchula konse ndi chitamando chilichonse! Chimene chaululidwa ndi Inu ndikhumbo la mtima wanga ndiponso chokondedwa cha moyo wanga. “O Mulungu, Mulungu wanga! Musaone zimene ndifuna ndi zochita zanga koma muone chifuniro Chanu zimene zakutila kumwamba ndi pansi pano. Mu Dzina Lanu Lalikulu Lopambana kwambiri, O Inu Ambuye wa mafuko onse! Ndikufuna zokha zimene Inu mufuna, ndipo zokha zimene Inu Mukonda.”

Kenaka iye agwade, ndikugwetsa mphumi yake pansi, anene kuti:

Okwezeka Muli Inu pamwamba pa chifotokozo cha wina aliyense kupatula Inu nokha, ndi kuzindikirika ndi kena kalikonse kupatula Inu.

Kenaka ayimilire ndi kunena:

“Pangani pemphero langa, O Ambuye wanga, mtsinje wa madzi a moyo pamene ndingathe kukhala moyo wautali monga m’mene ufumu Wanu ungakhalire, ndipo

ndingathe kutchula Inu mudziko liri lonse la Maiko Anu." Kenaka iye akwezenso manja ake mopempha, ndipo anene:

O Inu amene polekanitsidwa Nanu mitima ndi miyoyo yosungunuka, amenenso ndi moto wa chikondi Chake dziko lonse lapansi layatsidwa! Ndikudandaulira Inu mwa Dzina Lanu kubzolera mwa lomwe Inu mwagonjetsa chilengedwe chonse, musandimane ine chimene chilli ndi Inu, O Inu Amene mulamulira anthu onse! Inu mukumuona, O Ambuye wanga, mlendoyu kuthawira kwawo kokwezeka kopambana pansi pa chophimba cha ufumu Wanu, ndi cholengedwa chosaukachi kasupe wa chuma Chanu. Yanu ndi mphamvu yolamulira chilichonse chomwe Inu mufuna. Ndichitira umboni kuti Inu muyenera kutamandidwa mu zochita Zanu, ndi kukumverani mu chilamulo Chanu, ndi kukhalabe osakakamizidwa mu ulamuliro Wanu.

Kenaka a kweze manja ake ndi kunena Dzina Lalikulu (Alláh-u-Abhá) katatu.

Kenaka aweramire pansi manja ali pa maondo pamaso pa Mulungu – wodalitsika ndi okwezeka akhale Iye – ndi kunena:

Inu mukuona, O Mulungu wanga, momwe mzimu wanga wagwedezekera mkati mwa nthiti ndi ziwalo zanga, mkufunitsitsa kwake kuti ukupembedzeni Inu, ndi mkulakalaka kwake kuti ukukumbukireni Inu ndi kukulemekezani Inu; momwe ukuchitira umboni mu ufumu wa chinenero Chanu ndi kumwamba kwa Nzeru Zanu. Ndikonda mu khalidwe limeneli, O Ambuye wanga, kupempha kwa Inu zonse zimene muli nazo, kuti ndilangize umphawi wanga, ndi kukulitsa chaulere Chanu ndi chuma Chanu, ndi kulengeza kufooka kwanga, ndi kuvumbula mphamvu Zanu ndi Nyonga Zanu.

Kenaka iye ayimirire ndi kukweza manja ake kawiri mopempha, ndi kunena:

Kulibe Mulungu wina koma Inu, Wamphamvu zonse, wachaulere Chonse. Kulibe Mulungu koma Inu, mkozi, poyamba ndi pomaliza pomwe. O Mulungu, Mulungu wanga! Chikhululuko Chanu chandilimbikitsa, ndipo kuyitana kwanu kwandidzutsa, ndipo chisomo chanu chandikweza ndi kunditsogolera kwa Inu. Ndine yani, kuti ndingathe kulimba mtima kuti ndiyimilire pachipata cha mzimu woyandikira Nanu, kapenanso kulodzetsa nkhope yanga ku nyali zomwe zili kuwala kuchokera kumwamba kwa chifuniro chanu? Inu mukuona, O Ambuye wanga, cholengedwa chochititsa chisonichi chikugogoda pakhomo lachisomo Chanu, ndi moyo wakuthawu ukufunafuna mtsinje wamoyo osatha kuchokera kumanja a chaulere Chanu. Chanu ndi chilamulo nthawi zonse, O Inu Amene muli Ambuye wa maina onse, ndipo kwanga ndi kusawiringula ndi kugonjera malolera ku chifuniro Chanu, O Mlengi wa miyamba!

Kenaka iye akweze manja ake katatu ndi kunena:

Wamkulu ndi Mulungu kuposa wamkulu aliyense!

Kenaka iye agwade ndi kugwetsa mphumi yake pansi, ndi kunena:

Muli apamwamba zedi Inu kukutamandani kwa iwo amene ali pafupi Nanu kuti afike kumwamba pafupi Nanu, kapena mbalame za mitima ya iwo amene ali odzipereka kwa Inu kuti afikedi pa chitseko cha chipata chanu. Ndichitira umboni kuti Muli opatulika pamwamba pa zizindikiro zonse, ndiponso Woyera pamwamba pa maina onse. Palibe Mulungu wina koma Inu, wopambana koposa onse, wa Ulemerero onse.

Kenaka akhazikike pansi ndi kunena:

Ndichitira umboni ku chimene zolengedwa zonse zachitira umboni, ndi makamu a kumwamba, ndi okhala mu Paradizo Okwezeka koposa, ndipo kuseri kwaoko lilime la ulemelero ili lomwe kuchokera ku malekezero a ulemelero onse, kuti Ndinu Mulungu, kuti kulibenso Mulungu koma Inu, ndipo kuti Iye Amene wavumbulutsidwa ndi chinsinsi chobisika, chizindikiro chosungidwa, kubzolera mwa Amene malembo B ndi E (kukhala) aphatikizana ndi kulukana pamodzi. Ndichitira umboni kuti ndi Iyeyo Amene dzina lake lalembedwa ndi Cholembera cha Wamwambamwamba, ndinso Amene watchulidwa mu Mabuku a Mulungu, Ambuye Wampando wa Chifumu m’mwambamo ndi pansi pano. Kenaka ayimilire njo ndi kunena:

O Ambuye wa zolengedwa zonse ndi mwini wa zinthu zonse zooneka ndi zosaoneka! Inu mukuiona misozi yanga ndi zisisimo zomwe ndikunena, ndi kumvetsera ku kubuula kwanga, ndi kuchema ndi chiliro cha mtima wanga. Ndi nyonga Zanu! Zolakwa zanga zanditsekerezera kumbuyo kuti ndisayandikire Nanu; ndipo machimo anga andiyimitsa kutali kuchokera kubwalo la milandu la chiyero Chanu. Chikondi Chanu, O Ambuye wanga, chandilemeza ine, ndipo malekano ndi Inu yandiononga ine, kutalikirana ndi Inu kwandidya ine.

Ndikupemphani Inu ndi mayendedwe Anu mu chipululuchi, ndiponso ndi mawu “Ndili pano, Ndili pano” amene osankhidwa Anu adalankhula mu ufumu Wanu, ndi mpumo wa Chibvumbulutso Chanu, ndi mphepo zodekha za kudza kwa Mbandakucha wa Mbvumbulutsi Wanu, kukonza kuti ndiyang’anire pa kukongola Kwanu ndi kutsata chilichonse chomwe chilli mu Bukhu Lanu.

Kenaka iye anene Dzina Lalikulu (Alláh-u-Abhá) katatu ndi kuweramira pansi manja ali pa maondo, ndi kunena:

Mayamiko akhale kwa Inu, O Mulungu wanga, pakuti Inu mwandithandiza kukumbukira Inu ndiponso kukuyamikani Inu, ndipo mwandizindikiritsa ine Iye Amene ali Mbandakucha wa Zizindikiro Zanu, ndipo mwandipangitsa kuweramira pansi pamaso pa Umbuye Wanu, ndi kudzichepetsa pamaso pa Umulungu Wanu, ndi kuvomereza chimene chayankhulidwa ndi lilime la ukulu wanu.

Kenaka iye aweramuke ndi kunena:

O Mulungu, Mulungu wanga! Msana wanga wawelama ndi kulemedwa kwa machimo anga, ndipo kusasamala kwanga kwandiononga ine. Ndikamaganizira kuipa kwa zochita zanga ndi chisamaliro Chanu, mtima wanga usungunuka mkati mwanga, ndipo magazi anga akuwira mkati mwa misempha yanga. Mwa kukongola Kwanu, O Inu khumbo la Dziko lapansi! Ndili ndi manyazi kukweza nkhope yanga kwa inu, ndipo manja anga olakalaka ali ndi manyazi kutambasukira kuloza kumwamba kwa chaulere Chanu. Inu mukuona, O Mulungu wanga, momwe misozi yanga ikundilepheretsa kukumbukira Inu ndi kukuza zabwino Zanu, O Inu Ambuye Wampando wa Chifumu m’mwambamo ndi dziko lapansi pano!

Ndikudandaulirani mwa zizindikiro za Ufumu Wanu ndi zodabwitsa za ulamuliro Wanu kuchita ndi okondedwa Wanu monga kuyenera chaulere Chanu, O Ambuye wa zamoyo zonse, ndipo muyeneradi chisomo Chanu, O Mfumu ya zooneka ndi zosaoneka!

Kenaka iye anene Dzina lalikulu (Alláh-u-Abhá) katatu ndi kugwada mphumi yake ili pansi ndi kunena:

Mayamiko akhale kwa Inu, O Mulungu wathu, pakuti Inu mwatitumizira ife chomwe chatisendeza m’fupi ndi Inu, ndipo mutipatse ife chabwino chilichonse chotumizidwa ndi Inu mu Mabukhu Anu ndi Malembo Anu. Titetezeni, tikupemphani Inu, O Ambuye wanga, ku makamu a malingaliro a zinthu zopanda pake, ndi maganizo achabe.

Inu, ndithudi, Ndinu Wanyonga, Wodziwa Zonse.

Kenaka awutse mutu wake ndikukhazikika pansi ndi kunena:

Ndichitira umboni, O Mulungu wanga, kuchimene osankhidwa Anu achichitira umboni, ndi kuvomereza chimene okhala ku Paradizo okwezekayo ndi iwo azinga mozungulira mpando Wanu Wamphamvu achivomereza. Maufumu adziko lapansi ndi kumwamba ndi Anu, O Ambuye wa maiko!

Ulemerero ukhale kwa Inu, O Mbuye Mulungu wanga! Ndikupemphani Inu m’dzina Lanu. kupyolera mmene Iye Amene Ndiye kukongola Kwanu, wakhazikitsidwa pa ufumu wa Chipembedzo Chanu, ndipo ndi m’dzina Lanu kupyolera m’lomwero musintha zinthu zonse ndipo musonkhanitsa zinthu zonse pamodzi, ndi kuitana zinthu zonse ku bwalo ndikusupa zinthu zonse, ndi kuteteza zinthu zonse. Ndikupemphani Inu kulondera mdzakaziyu amene wathawira ku mpumulo Wanu ndipo wafunafuna mthunzi wa Amene mwa Iye Inu mwaonekeramo ndipo waika chikhulupiriro ndi chigomezero chake chonse mwa Inu.

Mdzakaziyu akudwala, O Mulungu wanga ndipo walowa kunsi kwa mthunzi wa Mtengo wa machiritso Anu, wokanthidwa, ndipo wathawira ku Mzinda wa chitetezo Chanu, wadwala, ndipo wafunafuna Mutu wa Kasupe wa kukoma mtima Kwanu; wobuwula ndi ululu, ndipo wakangazira kuti akapeze Chitsime cha Mweza wa kudekha Kwanu; walemedwa ndi tchimo, ndipo walunjikitsa nkhope yake ku bwalo la chikhululukiro Chanu.

Muvekeni iye, mwa ulamuliro Wanu ndiponso mwa chikondi cha kukoma mtima Kwanu, O Mulungu wanga ndi Wokondedwa wanga, ndi chovala cha chitonthozo ndi kuchiritsa Kwanu, ndipo mpangeni iye kumwera mu chikho cha chifundo ndi kukoma mtima Kwanu.

Mtetezeni iye, makamaka ku zovuta ndi zopweteka zonse, ku zowawa zonse ndi matenda ndiponso kuchokera ku chiri chonse choyipa kwa Inu.

Inu, m’chowonadi, Muli Wokwezeka kopambana pamwamba pa zonse kupatula Inu Mwini. Inu indetu, Ndinu Wochiza, Wokwaniritsa Zonse, Msungi, Wokhululukira, Wachifundo chopambana.

Mayamiko akhale kwa Inu, O Ambuye Mulungu wanga! Ndikupemphani Inu mwa Chibvumbulutso chomwechi chimene chasandutsa m’dima kukhala kuwala, kubzolera muchomwechi Kachisi Wanu wobwerezedwa10 bwerezedwa wamangidwa, ndipo Uthenga Wolembedwa waululidwa, ndi Kalata Yolalikidwa yamasulidwa kunditumizira ine ndi iwo amene ali ndi ine chimene chingatithandize kuuluka kunka kumwamba kwa ulemelero Wanu wopambana, ndikutitsuka ife litsilo la kusakhulupilira lomwe lalepheretsa okaika kulowa mu Kachisi wa umodzi Wanu.

Ine ndine, O Ambuye wanga, amene ndagwira molimba chingwe chachikondi Chanu, ndikukakamirira ku mpindiro wa chisomo ndi chifundo Chanu. Ndikonzereni ine pamodzi ndi okondedwa anga zabwino zadziko lino ndi zadziko limene liri m’kudza. Agawireni iwo, tsono mphatso Zobisika zimene Munawakonzera osankhidwa pakati pazolengedwa Zanu.

Tsono awa, O Ambuye wanga, ndimasiku amene mwawalamulira a ntchito Anu kusala kudya. Ngodala iye amene asala chakudya chifukwa cha Inu Nokha ndikudzipatula kotheratu kuzinthu zonse koma Inu Nokha. Ndithandizeni ine ndikuwathandiza iwo, O Ambuye wanga, kubvera Inu ndi kusunga malamulo Anu.

Inu, indetu, Muli ndi mphamvu yochita zomwe Mwasankha. Kulibe Mulungu wina koma Inu Nokha, Wodziwa zonse. Mayamiko onse akhale kwa Mulungu, Ambuye wa maiko onse.

Ulemelero ukhale kwa Inu, O Ambuye Mulungu wanga! Musanyasidwe naye iye amene Inu mwamkweza kupyolera mu mphamvu ya ufumu Wanu wamuyaya, ndi kumsiya kutali ndi Inu, amene Inu Munamlola kulowa m’chihema Chanu cha kunthawi zosatha. Kodi Mungamtaye, O Mulungu wanga iye amene Inu Mwamphimba ndi Ufumu Wanu ndipo mungamtembenukire, O chifuniro changa amene Mwakhala pothawira pake? Mungamunyoze iye amene Inu Mwamtukula, kapena Kumuiwala iye amene Inu munanthandiza kukukumbukirani? Wolemekezedwa, kwamtheradi Muli Wolemekezedwa Inu! Inu muli Amene kuyambira pachiyambi Mwakhala Mfumu ya chilengedwe chonse ndi Woyendetsa Wake ndipo mpaka ku nthawi zosatha Mudzakhalabe Ambuye wa zolengedwa zonse ndi Mkozi Wake.

Wolemekezedwa muli Inu, O Mulungu wanga! Ngati Muleka kuchitira chisoni antchito Anu, ndani nanga angawachitire chisoni? Ndipo ngati Mukana kudyetsa okondedwa Anu, kuli ndaninso woti angawadyetse? Wolemekezedwa, kwamtheradi Muli Wolemekezedwa

Inu! Inu Mulambiridwa m’choonadi Chanu, ndipo Inu ndithudi ife tonse tikupembedzani, ndipo Inu Muli woonekera m’chilungamo Chanu, ndipo kwa Inu tonse, ndithu tichitira umboni. Inu muli, mchoonadi, wokondedwa mchisomo Chanu. Palibe Mulungu wina koma Inu Wothandiza pa Tsoka, Wosasowa kanthu.

Likuzike Dzina Lanu, O Ambuye Mulungu wanga! Inu ndi Iye amene zinthu zonse zimpembedza ndi Amene sapembedza kanthu. Amene Ali Ambuye wa zinthu zonse ndipo Sali kapolo wa kanthu. Amene Adziwa zonse koma sadziwidwa ndi kanthu. Inu Munafuna kuzizindikiritsa Nokha kwa wanthu; choncho, kupyolera mwa liu lapakamwa panu munadzetsa chilengedwe ndi kupanga m’mwamba. Palibe Mulungu wina koma Inu Nokha, Mkozi, Mulengi, Wamkulukulu, Wamphamvu Zonse.

Ndikupemphani, mwa liu lomweli, limene lawala pamwamba pa mzere wa Chifuniro Chanu, mundilore ndimwe mokwanira, madzi amoyo amene mwatsitsimutsa nawo mitima ya wosankhidwa Anu ndi kuukitsa mizimu ya wokondedwa Anu, kuti ine nthawi zonse, m’zooneka zonse, nditembenukire nkhope yanga kwa Inu.

Inu Ndinu Mulungu Wamphamvu, Waulemelero ndi Chaulere. Kulibe Mulungu wina pambali Panu, Woweruza Wamkulu, Woyerayera, Wanzeru-zonse.

Ndichitira umboni, O Mulungu wanga, kuti Munandilenga ine, kuti ndikudziweni ndi kukupembedzani. Nditsimikizira, panthawi ino, kufooka kwanga ndi kukula kwa mphamvu Zanu, kusauka kwanga ndi kulemera Kwanu.

Kulibe Mulungu wina koma Inu, Wothandiza pa Tsoka, Wodzidalira Nokha.